22. Ndi Segubu anabala Yairi, amene anali nayo midzi makumi awiri mphambu itatu m'dziko la Gileadi.
23. Ndi Gesuri ndi Aramu analanda midzi ya Yairi, pamodzi ndi Kenati ndi miraga yace; ndiyo midzi makumi asanu ndi limodzi. Iwo onse ndiwo ana a Makiri atate wa Gileadi.
24. Ndipo atafa Hezroni m'Kalebi-Efrata, Abiya mkazi wa Hezroni anambalira Asini atate wa Tekoa.