1 Mafumu 7:41-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Nsanamira ziwirizo, ndi mbale za mitu inali pamwamba pa nsanamira ziwirizo, ndi maukonde awiri ophimbira mbale ziwiri za mitu inali pamwamba pa nsanamirazo,

42. ndi makangaza mazana anai a maukonde awiriwo, mizere iwiri ya makangaza a ukonde umodzi kuphimbira mbale ziwiri za mitu inali pa nsanamirazo,

43. ndi maphaka khumiwo ndi mbiya khumi ziri pa maphakawo,

44. ndi thawale limodzilo, ndi ng'ombe khumi mphambu ziwirizo pansi pa thawale;

1 Mafumu 7