1 Mafumu 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mfumu Solomo anali mfumu ya Israyeli yense.

2. Ndipo akuru a mfumu ndi awa: Azariya mwana wa Zadoki anali nduna,

3. Elihorepa ndi Ahiya ana a Sisa alembi, Yehosafati mwana wa Ahiludi wolembera mbiri,

4. ndi Benaya mwana wa Yehoyada anali kazembe wa nkhondo, ndi Zadoki ndi Abyatara anali ansembe,

1 Mafumu 4