1 Mafumu 18:33-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Ndipo anakonza nkhunizo, naduladula ng'ombe, naiika pankhuni. Nati, Dzazani madzi mbiya zinai, muwathire pa nsembe yopsereza ndi pankhuni.

34. Nati, Bwerezaninso kawiri; nabwerezanso. Nati, Bwerezani katatu; nabwereza katatu.

35. Ndipo madzi anayenda pozinga guwa la nsembe, nadzazanso meerawo ndi madzi.

1 Mafumu 18