25. Ndipo akafika munthu yense ndi mtulo wace, zotengera zasiliva, ndi zotengera zagolidi, ndi zobvala, ndi zida, ndi zonunkhira, ndi akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.
26. Ndipo Solomo anasonkhanitsa, magareta ndi apakavalo; anali nao magareta cikwi cimodzi mphambu, mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri, nawasungira m'midzi yosungamo magareta, ndi kwamfumu m'Yerusalemu.
27. Ndipo mfumu inacurukitsa siliva ngati miyala m'Yerusalemu, ndi mitengo yamikungudza anailinganiza ndi mikuyu ya m'madambo.