1 Akorinto 10:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

14. Cifukwa cace, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.

15. Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu cimene ndinena.

16. Cikho ca dalitso cimene tidalitsa, siciri ciyanjano ca mwazi wa Kristu kodi? Mkate umene tinyema suli ciyanjano ca thupi la Kristu kodi?

1 Akorinto 10