Zekariya 12:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala m'Yerusalemu, mzimu wa cisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wace mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wace woyamba.

11. Tsiku lomwelo kudzakhala maliro akuru m'Yerusalemu, ngati maliro a Hadadirimoni m'cigwa ca Megidoni,

12. Ndipo dziko lidzalira, banja liri lonse pa lokha; banja la nyumba ya Davide pa lokha, ndi akazi ao pa okha; banja la nyumba ya Natani pa lokha, ndi akazi ao pa okha;

13. banja la nyumba ya Levi pa lokha, ndi akazi ao pa lokha; banja la Asimei pa okha, ndi akazi ao pa okha;

Zekariya 12