8. Ndinamva kutonza kwa Moabu ndi matukwano a ana a Amoni, zimene anatonza nazo anthu anga, ndi kudzikuza pa malire ao.
9. Cifukwa cace, pali moyo wanga, ati Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, Zedi Moabu adzakhala ngati Sodomu, ndi ana a Amoni ngati Gomora, pocuruka khwisa ndi maenje a mcere, ndi bwinja losatha; otsala a anthu anga adzalanda zao, ndi otsala amtundu wa anthu anga adzawalandira akhale colowa cao.
10. Ici adzakhala naco m'malo mwa kudzikuza kwao, cifukwa anatonza, nadzikuza pa anthu a Yehova wa makamu.