Yoswa 19:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

22. ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.

23. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

Yoswa 19