Yoswa 19:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;

15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.

16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

Yoswa 19