1. Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wace ali m'mimba mwa nsombayo.
2. Ndipo anati,Ndinaitana Yehova m'nsautso yanga,Ndipo anandiyankha ine;Ndinapfuula ndiri m'mimba ya manda,Ndipo munamva mau anga.
3. Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja,Ndipo madzi anandizinga;Mapfunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.
4. Ndipo ndinati, Ndatayika ndicoke pamaso panu;Koma ndidzapenyanso Kacisi wanu wopatulika.
5. Madzi anandizinga mpaka moyo wanga,Madzi akuya anandizungulira,Kayandeyande wa m'nyanja anandikulunga mutu.
6. Ndinatsikira ku matsinde a mapiri,Mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha;Koma munandikwezera moyo wanga kuucotsa kucionongeko, Yehova Mulungu wanga.
7. Pokomoka moyo wanga m'kati mwanga ndinakumbukila Yehova;Ndi pemphero langa linafikira Inu m'Kacisi wanu wopatulika.
8. Iwo osamalira mabodza opanda paceAtaya cifundo cao cao.