33. Ngatiuyu sanacokera kwa Mulungu, sakadakhoza kucita kanthu.
34. Anayankha natikwa iye, Wabadwa iwe konse m'zoipa, ndipo iwe utiphunzitse ife kodi? Ndipo anamtaya kunja.
35. Yesu anamva kuti adamtaya kunja; ndipo pakumpeza iye, anati, Kodi ukhulupirira Mwana wa Mulungu?
36. Iyeyu anayankha nati, Ndipo ndani iye, Ambuye, kuti ndimkhulupirire iye?