22. Izi ananena atate wace ndi amace, cifukwa anaopa Ayuda; pakuti Ayuda adapangana kale, kuti ngati munthu ali yense adzambvomereza iye kuti ndiye Kristu, akhale woletsedwa m'sunagoge,
23. Cifukwa ca ici atate wace ndi amace anati, Ali wamsinkhu; mumfunse iye.
24. Pamenepo anamuitana kaciwiri munthuyo amene anali wosaona, nati kwa iye, Lemekeza Mulungu; tidziwa kuti munthuyo ali wocimwa.
25. Pamenepo iyeyu anayankha, Ngati ali wocimwa, sindidziwa; cinthu cimodzi ndicidziwa, pokhala ndinali wosaona, tsopano ndipenya.
26. Cifukwa cace anati kwa iye, Anakucitira iweciani? anakutsegulira iwe maso bwanji?
27. Iye anayankha iwo, Ndinakuuzani kale, ndipo simunamva; mufuna kumvanso bwanji? kodi inunso mufuna kukhala: akuphunzira ace?