Yohane 9:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Izi ananena atate wace ndi amace, cifukwa anaopa Ayuda; pakuti Ayuda adapangana kale, kuti ngati munthu ali yense adzambvomereza iye kuti ndiye Kristu, akhale woletsedwa m'sunagoge,

23. Cifukwa ca ici atate wace ndi amace anati, Ali wamsinkhu; mumfunse iye.

24. Pamenepo anamuitana kaciwiri munthuyo amene anali wosaona, nati kwa iye, Lemekeza Mulungu; tidziwa kuti munthuyo ali wocimwa.

25. Pamenepo iyeyu anayankha, Ngati ali wocimwa, sindidziwa; cinthu cimodzi ndicidziwa, pokhala ndinali wosaona, tsopano ndipenya.

Yohane 9