43. 5 Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo cifukwa ca iye.
44. Koma 6 ena mwa iwo anafuna kumgwira iye; koma palibe munthu anamgwira kumanja.
45. Pamenepo anyamatawo anadza kwa ansembe akulu ndi Afarisi; ndipo iwowa anati kwa iwo, Simunamtenga iye bwanji?
46. Anyamatawo anayankha, 7 Nthawi yonse palibe munthu analankhula cotero.
47. Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?
48. 8 Kodi wina wa akuru anakhulupirira iye, kapena wa Afarisi?
49. Koma khamu ili losadziwa cilamulo, likhala lotembereredwa.
50. 9 Nikodemo ananena kwa iwo, amene uja adadza kwa iye kale, ali mmodzi wa iwo,
51. Kodi cilamulo cathu ciweruza munthu, osayamba kumva iye, ndi kuzindikira cimene, acita?