48. Pamenepo Yesu anati kwa iye, Ngati simuona zizindikilo ndi zozizwa, simudzakhulupira.
49. Mkuluyo ananena kwa iye, Ambuye, tsikani asanafe mwana wanga.
50. Yesu ananena naye, Muka, mwana wako ali ndi moyo, Munthuyo anakhulupirira mau amene Yesu anatero naye, namuka.
51. Ndipo m'mene analikutsika, akapolo ace anakomana, naye, nanena, kuti, Mwana wanu ali ndi moyo.