30. Anaturuka iwo m'mudzi ndipo analinkudza kwa iye.
31. Pa mphindikati iyi ophunzira ace anampempha iye, ndi kunena, Rabi, idyani.
32. Koma iye anati kwa iwo, Ine ndiri naco cakudya cimene inu simucidziwa.
33. Cifukwa cace ophunzira ananena wina ndi mnzace, Kodi pali wina anamtengera iye kanthu kakudya?