Yohane 4:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. (angakhale Yesu sanabatiza yekha koma ophunzira ace),

3. anacokera ku Yudeya, namukanso ku Galileya.

4. Ndipo anayenerakupita pakati pa Samariya.

5. Cifukwa cace anadza ku mudzi wa Samariya, dzina lace Sukari, pafupi pa kadziko kamene Yakobo adapatsa mwana wace Yosefe;

6. ndipo pamenepo panali citsime ca Yakobo. Ndipo Yesu, popeza analema ndi ulendo wace, motero anakhala pacitsime,

Yohane 4