Yohane 4:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa cace pamene Ambuye anadziwa kuti Afarisi adamva kuti Yesu anayesa anthu ophunzira, nawabatiza koposa Yohane

2. (angakhale Yesu sanabatiza yekha koma ophunzira ace),

3. anacokera ku Yudeya, namukanso ku Galileya.

4. Ndipo anayenerakupita pakati pa Samariya.

5. Cifukwa cace anadza ku mudzi wa Samariya, dzina lace Sukari, pafupi pa kadziko kamene Yakobo adapatsa mwana wace Yosefe;

6. ndipo pamenepo panali citsime ca Yakobo. Ndipo Yesu, popeza analema ndi ulendo wace, motero anakhala pacitsime,

7. Kunali ngati ora lacisanu ndi cimodzi. Kunadza mkazi woturuka m'Samariya kudzatunga madzi. Yesu ananena naye, Undipatse Ine ndimwe.

8. Pakuti ophunzira ace adacoka kunka kumudzi kuti akagule cakudya.

Yohane 4