Yohane 3:32-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Cimene anaciona nacimva, acita umboni wa ici comwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wace.

33. 1 Iye amene analandira umboni wace anaikapo cizindikilo cace kuti Mulungu ali woona.

34. Pakuti 2 Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti 3 sapatsa Mzimu ndi muyeso.

35. 4 Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lace.

36. Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.

Yohane 3