Yohane 3:28-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Inu nokha mundicitira umboni, kuti ndinati, Sindine Kristu, koma kuti ndiri wotumidwa m'tsogolo mwace mwa iye.

29. Iye amene ali naye mkwatibwi ali mkwati, koma mnzace wa mkwatiyo, wakuimirira ndi kumvera iye, akondwera kwakukuru cifukwa ca mau a mkwatiyo; cifukwa cace cimwemwe canga cimene cakwanira.

30. Iyeyo ayenera kukula koma ine ndicepe.

31. Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse; iye amene ali wa dziko lapansi ali wa dziko lapansi, nalankhula za dziko lapansi: Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse.

32. Cimene anaciona nacimva, acita umboni wa ici comwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wace.

33. 1 Iye amene analandira umboni wace anaikapo cizindikilo cace kuti Mulungu ali woona.

34. Pakuti 2 Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti 3 sapatsa Mzimu ndi muyeso.

35. 4 Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lace.

36. Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.

Yohane 3