39. Anafunanso kumgwira iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.
40. Ndipo anacoka kunkanso tsidya lija la Yordano, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.
41. Ndipo ambiri anadza kwa iye; nanena kuti, Sanacita cizindikilo Yohane; koma zinthu ziri zonse Yohane ananena za iye zinali zoona.
42. Ndipo ambiri anakhulupirira iye komweko.