Yohane 10:39-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Anafunanso kumgwira iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.

40. Ndipo anacoka kunkanso tsidya lija la Yordano, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.

41. Ndipo ambiri anadza kwa iye; nanena kuti, Sanacita cizindikilo Yohane; koma zinthu ziri zonse Yohane ananena za iye zinali zoona.

42. Ndipo ambiri anakhulupirira iye komweko.

Yohane 10