19. Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda cifukwa ca mau awa.
20. Koma ambiri mwa iwo ananena, Ali ndi ciwanda, nacita misala; mukumva iye bwanji?
21. Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa ciwanda. Kodi ciwanda cikhoza kumtsegulira maso wosaona?
22. Koma kunali phwando la kukonzersanso m'Yerusalemu; nyengoyo ndi yacisanu.
23. Ndipo Yesu analikuyendayenda m'Kacisi m'khumbi la Solomo,
24. Pamenepo Ayuda anamzungulira iye, nanena ndi iye, Kufikira liti musfnkhitsa-slnkhitsa moyo wathu? ngati Inu ndinu Kristu, tiuzeni momveka.