24. Ndipo otumidwawo analia kwa Marisi.
25. Ndipo anamfunsa iye, nati kwa iye, Koma ubatiza bwanji, ngati suli Kristu, kapena Eliya, kapena Mneneriyo?
26. Yohane anawayankha, nati, 2 Ine ndibatiza ndi madzi; pakati pa inu paimirira amene simumdziwa,
27. 3 ndiye wakudza pambuyo panga, amene sindiyenera kummasulira lamba la nsapato yace.