Yohane 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. PACIYAMBI panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

2. Awa anali paciyambi kwa Mulungu,

3. Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,

4. Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.

5. Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.

6. Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.

Yohane 1