Yobu 8:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono,Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.

8. Pakuti ufunsire tsono mbadwo wapitawo,Nusamalire zimene makolo ao adazisanthula;

9. Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu,Popeza masiku athu a pa dziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;

10. Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera,Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?

Yobu 8