15. Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira;Adzaiumirira koma yosakhalitsa.
16. Akhala wamuwisi pali dzuwa,Ndi nthambi zace ziturukira pamunda pace.
17. Mizu yace iyangayanga pa kasupe wamadzi,Apenyerera pokhalapo miyala.
18. Akamuononga kumcotsa pamalo pace,Padzamkana, ndi kuti, Sindinakuona.