Yobu 8:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera,Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?

11. Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho?Ngati mancedza amera popanda madzi?

12. Akali auwisi, sanawaceka,Auma, asanaume mathengo onse ena.

13. Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu;Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;

14. Kulimbika mtima kwace kudzatyoka,Cikhulupiriro cace cikunga nyumba ya tandaude.

15. Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira;Adzaiumirira koma yosakhalitsa.

Yobu 8