Yobu 6:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!

9. Cimkomere Mulungu kundiphwanya,Alole dzanja lace lindilikhel

10. Pamenepo ndidzasangalala,Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka;Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.

11. Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?

12. Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?

Yobu 6