5. Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?
6. Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere?Coyera ca dzira cikolera kodi?
7. Zimene moyo wanga ukana kuzikhudzaZikunga cakudya cosakolera kwa ine.
8. Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!
9. Cimkomere Mulungu kundiphwanya,Alole dzanja lace lindilikhel
10. Pamenepo ndidzasangalala,Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka;Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.
11. Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?