12. Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?
13. Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.
14. Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.
15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.