Yobu 6:11-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?

12. Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?

13. Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.

14. Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.

15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.

16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;

17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.

18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.

19. Aulendo a ku Tema anapenyerera,Makamu a ku Seba anaiyembekezera.

20. Anazimidwa popeza adaikhulupirira;Anafikako, nathedwa nzeru.

21. Pakuti tsopano mukhala mamwemo;Muona coopsa, mucitapo mantha.

22. Ngati ndinati, Mundipatse?Kapena, Muperekeko kwa ine cuma canu?

23. Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani?Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?

24. Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.

25. Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?

26. Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.

27. Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.

28. Koma tsopano balindani, mundipenyerere;Ndikanena bodza pamaso panu mudzalizindikira.

Yobu 6