Yobu 6:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?

12. Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?

13. Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.

14. Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.

15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.

16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;

17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.

18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.

Yobu 6