10. Amene abvumbitsa mvula panthaka,Natumiza madzi paminda;
11. Kuika opeputsidwa pamalo ponyamuka,Kuti iwo a maliro akwezedwe posatekeseka.
12. Apititsa pacabe ziwembu za ocenjerera,Kuti manja ao sakhoza kucita copangana cao.
13. Akola eni nzeru m'kucenjerera kwao,Ndi uphungu wa opotoka mtima usonthokera pacabe,