Yobu 42:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Yobu anayankha Mulungu, nati,

2. Ndidziwa kuti mukhoza kucita zonse,Ndi kuti palibe coletsa colingirira canu ciri conse,

3. Ndani uyu abisa uphungu wosadziwa kanthu?Cifukwa cace ndinafotokozera zimene sindinazizindikira,Zondidabwiza, zosazidziwa ine,

4. Tamveranitu, ndidzanena ine,Ndidzakufunsani, mundidziwitse.

5. Kumva ndidamva mbiri yanu,Koma tsopano ndikupenyani maso;

Yobu 42