Yobu 40:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pamenepo Yobu anayankha Yehova, nati,

4. Taonani, ndakhululuka ine, ndidzakubwezerani mau otani?Ndigwira pakamwa.

5. Ndalankhula kamodzi, koma sindidzayankha;Inde kawiri, koma sindionjezanso.

6. Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,

7. Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna;Ndidzakufunsa, undidziwitse.

8. Cingakhale ciweruzo canga udzacityola kodi?Udzanditsutsa kuti ndiri woipa kodi, kuti ukhale wolungama ndiwe?

Yobu 40