Yobu 40:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Tapenya tsono, mphamvu yace iri m'cuuno mwace,Ndi kulimbalimba kwace kuli m'mitsempha ya m'mimba yace.

17. Igwedeza mcira wace ngati mkungudza;Mitsempha ya ncafu zace ipotana.

18. Mafupa ace akunga misiwe yamkuwa;Ziwalo zace zikunga zitsulo zamphumphu,

19. Iyo ndiyo ciyambi ca macitidwe a Mulungu;Wakuilenga anaininkha lupanga lace.

20. Pakuti mapiri aiphukitsira cakudya,Kumene zisewera nyama zonse za kuthengo,

21. Igona pansi patsinde pa mitengo yamthunzi,Pobisala pabango ndi pathawale.

Yobu 40