Yobu 4:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Monga umo ndaonera, olimira mphulupulu,Nabzala bvuto, akololapo zomwezo.

9. Atayika ndi mpweya wa Mulungu,Nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wace.

10. Kubangula kwa mkango, ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa,Ndi mano a misona ya mkango atyoledwa.

11. Mkango wokalamba udzifera posowa mkoka,Ndi misona ya mkango waukazi imwazika.

12. Anditengera mau m'tseri,M'khutu mwanga ndinalandira kunong'oneza kwace.

13. M'malingaliro a masomphenya a usiku,Powagwira anthu tulo tatikuru,

Yobu 4