8. Monga umo ndaonera, olimira mphulupulu,Nabzala bvuto, akololapo zomwezo.
9. Atayika ndi mpweya wa Mulungu,Nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wace.
10. Kubangula kwa mkango, ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa,Ndi mano a misona ya mkango atyoledwa.
11. Mkango wokalamba udzifera posowa mkoka,Ndi misona ya mkango waukazi imwazika.
12. Anditengera mau m'tseri,M'khutu mwanga ndinalandira kunong'oneza kwace.
13. M'malingaliro a masomphenya a usiku,Powagwira anthu tulo tatikuru,