5. Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka;Cikukhudza, ndipo ubvutika.
6. Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu,Ndi ciyembekezo cako si ndiwo ungwiro wa njira zako?
7. Takumbukila tsopano, watayika ndani wosaparamula konse?Kapena oongoka mtima alikhidwa kuti?
8. Monga umo ndaonera, olimira mphulupulu,Nabzala bvuto, akololapo zomwezo.