Yobu 4:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu?Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?

18. Taona, sakhulupirira atumiki ace;Nawanenera amithenga ace zopusa;

19. Kopambana kotani nanga iwo akukhala m'nyumba zadothi,Amene kuzika kwao kuti m'pfumbi,Angothudzulidwa ngati gulugufe,

20. Kuyambira m'mawa kufikira madzulo athudzuka;Aonongeka kosatha, osasamalirako munthu.

21. Kukometsetsa kwao sikumacotsedwa nao?Amafa koma opanda nzeru.

Yobu 4