21. Apalasa kucigwa, nakondwera nayo mphamvu yace;Aturuka kukomana nao eni zida.
22. Aseka mantha osaopsedwa,Osabwerera kuthawa lupanga.
23. Phodo likuti koco koco panthiti pace,Mkondo wonyezimira ndi nthungo yomwe.
24. Ndi kunjenjemera kwaukali aimeza nthaka,Osaimitsika pomveka lipenga.