Yobu 38:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Kodi ungamange gulu la Nsangwe?Kapena kumasula zomangira za Akamwiniatsatana?

32. Ungaturutse kodi nyenyezi m'nyengo zao monga mwa malongosoledwe ao?Kapena kutsogolera Mlalang'amba ndi ana ace?

33. Kodi udziwa malemba a kuthambo?Ukhoza kukhazikitsa ufumu wao pa dziko lapansi?

34. Kodi udziwa kukwezera mau ako kumitambo,Kuti madzi ocuruka akukute?

Yobu 38