15. Kodi mudziwa umo Mulungu azilangizira zimenezi,Nawalitsa mphezi ya m'mtambo mwace?
16. Kodi mudziwa madendekeredwe ace a mitambo,Zodabwiza za Iye wakudziwa mwangwiro?
17. Kodi mudziwa umo zobvala zanu zifundira,Pamene dziko liri thuu cifukwa ca mwela?
18. Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye,Ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?