Yobu 36:26-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Taonani, Mulungu ndiye wamkuru, ndipo sitimdziwa;Ciwerengo ca zaka zace ncosasanthulika.

27. Pakuti akweza madontho a mvula,Akhetsa mvula ya m'nkhungu yace

28. Imene mitambo itsanulira,Nibvumbitsira anthu mocuruka.

29. Pali munthu kodi wodziwitsa mayalidwe a mitambo,Ndi kugunda kwa msasa wace?

30. Taonani, Iye ayala kuunika kwace pamenepo.Nabvundikira kunsi kwace kwa nyanja.

31. Pakuti aweruza nazo mitundu ya anthu.Apatsa cakudya cocuruka.

32. Akutidwa manja ace ndi mphezi,Nailamulira igwere pofunapo Iye.

Yobu 36