Yobu 36:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Apulumutsa wozunzika mwa kuzunzika kwace,Nawatsegulira m'khutu mwao mwa kupsinjika kwao.

16. Inde akadakukopani mucoke posaukira,Mulowe kucitando kopanda copsinja;Ndipo zoikidwa pagome panu zikadakhala zonona ndithu.

17. Koma mukadzazidwa nazo zolingirira oipa,Zolingirirazo ndi ciweruzo zidzakugwiranibe,

18. Pakuti mucenjere, mkwiyo ungakunyengeni mucite mnyozo;Ndipo usakusokeretseni ukulu wa dipoli.

19. Cuma canu cidzafikira kodi, kuti simudzakhala wopsinjika,Kapena mphamvu yanu yonse yolimba?

Yobu 36