28. Koma anandiombola ndingatsikire kumanda,Ndi moyo wanga udzaona kuunika.
29. Taona, izi zonse azicita MulunguKawiri katatu ndi munthu,
30. Kumbweza angalowe kumanda,Kuti kuunika kwa moyo kumuwalire.
31. Cherani khutu, Yobu, mundimvere ine;Mukhale cete, ndipo ndidzanena ine.
32. Ngati muli nao mau mundiyankhe.Nenani, pakuti ndifuna kukulungamitsani.