Yobu 33:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Amanga mapazi anga m'zigologolo,Ayang'anira poyenda ine ponse.

12. Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama;Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.

13. Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji?Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.

14. Pakuti Mulungu alankhula kamodzi,Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.

15. M'kulota, m'masomphenya a usiku,Pakuwagwera anthu tulo tatikuru,Pogona mwacheru pakama,

16. Pamenepo atsegula makutu a anthu,Nakomera cizindikilo cilangizo cao;

17. Kuti acotse munthu ku cimene akadacita,Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;

18. Kuti amletse angaonongeke,Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.

19. Alangidwanso ndi zowawa pakama pace,Ndi kulimbana kowawa kosapuma m'mafupa ace.

Yobu 33