10. Cifukwa cace ndinati, Ndimvereni ine,Inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.
11. Taonani, ndinalindira mau anu,Ndinacherera khutu zifukwa zanu,Pofunafuna inu ponena.
12. Inde ndinasamalira inu;Koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu,Kapena wakumbwezera mau pakati painu.
13. Msamati, Tapeza nzeru ndife,Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;
14. Popeza sanandiponyera ine mau,Sindidzamyankha ndi maneno anu.
15. Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.