Yobu 32:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Cifukwa cace ndinati, Ndimvereni ine,Inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.

11. Taonani, ndinalindira mau anu,Ndinacherera khutu zifukwa zanu,Pofunafuna inu ponena.

12. Inde ndinasamalira inu;Koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu,Kapena wakumbwezera mau pakati painu.

13. Msamati, Tapeza nzeru ndife,Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;

14. Popeza sanandiponyera ine mau,Sindidzamyankha ndi maneno anu.

15. Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.

Yobu 32