8. Ndibzale ine nadye wina,Ndi zondimerera ine zizulidwe.
9. Ngati mtima wanga wakopeka ndi mkazi,Ngati ndalalira pa khomo la mnzanga,
10. Mkazi wanga aperere wina;Wina namuike kumbuyo.
11. Pakuti ico ndi coipitsitsa,Ndico mphulupulu yoyenera oweruza anene mlandu wace.
12. Pakuti ndico moto wakunyeka mpaka cionongeko,Ndi cakuzula zipatso zanga zonse.