Yobu 31:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ngati ndalambira dzuwa lirikuwala,Kapena mwezi ulikuyenda monyezimira;

27. Ndi mtima wanga wakopeka m'tseri,Ndi pakamwa panga padapsompsona dzanja langa;

28. Icinso ndi mphulupulu yoyenera oweruza kunena mlandu wace;Pakuti ndikadakana Mulungu ali m'mwamba.

29. Ngati ndakondwera nalo tsoka la wondida,Kapena kudzitukula pompeza coipa;

30. Ndithu sindinalola m'kamwa mwanga mucimwe,Kupempha motemberera moyo wace.

Yobu 31